Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Mfumu yayikulu Mwirang’ombe yayamikira sukulu ya ntchito zaluso lamanja ku Karonga

Achinyamata a mdela la Mfumu yaikulu Mwirang’ombe ku Wovwe m’boma la Karonga awayamikira chifukwa chokhala ndi chidwi kuti aphunzire ntchito zaluso la manja mdelari.

Mfumu ya delari yanena izi pomwe achinyamata 90 alandira masatifiketi atatsiliza maphunziro awo, poonjezera kuti asonyeza chidwi chofuna kukhala nzika zodalirika.

Mkulu oyendetsa ntchito za bungwe lomwe limayang’anira maphunziro a ntchito zoterezi la TEVETA mchigawo chakumpoto a Joseph Chikopa auza MBC kuti ndizosangalatsa kuti nzika zamdela la Wovwe zikupindula zitagwirizana zoyitanitsa sukukuyi.

Wapampando wakhonsolo yaboma la Karonga a Bellium Msukwa anati ndiokondwa ndi sukuluyi ndipo anati aonetsetsa kuti apemphe khonsolo yawo kuti ikonze maofesi akale azaulimi a Wovwe omwe akungokhala kuti awakonzenso kuti akhale sukulu yokhazikika yantchito zaluso lamanja.

 

Olemba: Henry Haukeya

Related posts

GLOBAL FUND DONATES 41 UTILITY VEHICLES TO MIN OF HEALTH

MBC Online

Ekhaya three points behind leaders

Romeo Umali

Ministry of Local Govt urges councils to accelerate project implementation

McDonald Chiwayula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.