Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

MBC ikuchita bwino — Chiyamwaka

Unduna wazofalitsa nkhani wati ndiokhutira ndi m’mene MB ikugwirira ntchito zake  pokwaniritsa zokhumba za aMalawi onse m’dziko muno.

Mlembi wamkulu mu undunawu, a Baldwin Chiyamwaka, ati ndizosangalatsa kuti madandaulo amene anthu mmbuyomu anali nawo pa mapologalamu a MBC tsopano anachepa kwambiri, kutanthauza kuti bungweli likuyesetsa.

A Chiyamwaka anena izi atayendera maofesi a MBC ku Blantyre ndikuona zipangizo zomwe MBC ikugwiritsa ntchito powulutsa mawu.

Iwo ati undunawu upitiriza kuthandiza MBC munjira zosiyanasiyana kuti ikwaniritse zolinga zake zofikira aMalawi onse.

 

Related posts

MEC DECLARES GWENGWE WINNER, QUASHES COMPLAINTS FROM COMPETITOR

MBC Online

CHAKWERA ARRIVES IN EGYPT FOR COP27

Blessings Kanache

ISAMA commends MANEB for early release of examination results

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.