Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

MBC ikuchita bwino — Chiyamwaka

Unduna wazofalitsa nkhani wati ndiokhutira ndi m’mene MB ikugwirira ntchito zake  pokwaniritsa zokhumba za aMalawi onse m’dziko muno.

Mlembi wamkulu mu undunawu, a Baldwin Chiyamwaka, ati ndizosangalatsa kuti madandaulo amene anthu mmbuyomu anali nawo pa mapologalamu a MBC tsopano anachepa kwambiri, kutanthauza kuti bungweli likuyesetsa.

A Chiyamwaka anena izi atayendera maofesi a MBC ku Blantyre ndikuona zipangizo zomwe MBC ikugwiritsa ntchito powulutsa mawu.

Iwo ati undunawu upitiriza kuthandiza MBC munjira zosiyanasiyana kuti ikwaniritse zolinga zake zofikira aMalawi onse.

 

Related posts

Chipala, Kamwendo awonetse ukadaulo wawo — Chemis

Romeo Umali

Remnant Lions Theatre Group to premier “Belinda”

Rabson Kondowe

Amuna ambiri kumpoto akudwala khansa ya chida cha abambo

Alinafe Mlamba
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.