Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Amuna ambiri kumpoto akudwala khansa ya chida cha abambo

Akuluakulu apa chipatala chachikulu cha Mzuzu ati chipatalachi chikulandira abambo pafupifupi 60 mwezi uli ofuna chithandizo cha nthenda ya khansa ya chida cha abambo, penile cancer mchingerezi.

Malinga ndi Dr Alex Khombedza yemwe amayang’anira ntchito zamdulidwe pa chipatalachi, ambiri mwa abambowa ndi ochokera mzipatala zosiyanasiyana m’chigawo chakumpoto ndipo amafika zinthu zitaonongeka kale kaamba koti nthendayi imayamba ndi timatuza tomwe timanka tikula kutsogolo kwa chida cha abambo.

Dr Alex Khombedza, Mzuzu Central Hospital

Pa tsiku, chipatalachi chimalandira odwala matendawa awiri kapena atatu ndipo Dr Khombedza ati mdulidwe ndi njira yomwe ingathandize polimbana ndi vutoli.

Iwo amalankhula pamaphunziro a olembankhani m’chigawo chakumpoto amene anakonza ndi bungwe la JournAids linakonza ku Mzuzu.

Olembankhani omwe anatenga nao gawo pa maphunzirowa

Pakanali pano katswiri pa nkhani za umoyo George Jobe wati mpofunika kuti ma uthenga okhudza nthendayi afikile pali ponse pofuna kuteteza abambo ambiri ku nthendayi.

Related posts

‘Osagwiritsa ntchito imfa ya malemu Dr Chilima pa zifukwa za ndale’

Romeo Umali

Malawi ndi bwenzi lenileni la dziko la Zambia — Lufuma

Mayeso Chikhadzula

Masamba ndi Tcheta afwafwanthana madzulo ano

Alinafe Mlamba
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.