Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Sports Sports

‘Masewero opalasa njinga ali ndi tsogolo’

Unduna wa zamasewero wati ndi okondwa ndi luso limene laoneka pa mpikisano opalasa njinga ku Lilongwe, pamene bungwe la African Union Sports Council of Region 5 likukondwelera kuti lakwanitsa zaka 25.

Mlembi mu undunawu, a Chikumbutso Mtumodzi, anati boma liyesetsa kuthandiza masewerowa kudzera ku bungwe lowayendetsa la Cycling Federation of Malawi.

A Mtumodzi anati izi zili chomwechi chifukwa awona kuti masewerowa ali ndi tsogolo lowala ngati patakhala chidwi cha chikulu chowatukula kuchokera ku makampani komanso anthu osiyanasiyana akufuna kwabwino.

Pampikisanowu, a Peter Zulu ndi amene apambana atapalasa njinga pa mtunda wa makilomita 100 ndipo walandira mphotho yaikulu ya K600, 000.

A Rashid Aufi wakhala kwatswiri pa mtunda wa makilomita 50 ndipo walandira K300, 000.

Olemba: Batuel Gerald

Related posts

Nkhonya ya Hannock Phiri ndi Regene Champion ikununkhira

Romeo Umali

Empower women, girls with disabilities — FEDOMA

Romeo Umali

IPMM to tackle contemporary HR strategies

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.