Malawi Broadcasting Corporation
Development Local News Nkhani

Khonsolo ya Mzuzu ikufuna K2.4BN

Khonsolo ya mzinda wa Mzuzu yati ikufuna kutolera ndalama zokwana K2.4 billion kuti igwire bwino ntchito zake zachitukuko,pansi pa ndondomeko yake ya chuma ya 2024/2025.

Mkulu wa khonsoloyi, a Gomezgani Nyasulu, amayankhula izi pokhazikitsa ntchito za chitukukozi.

“Ndalama izizi zitithandiza kuti tipange zambiri, kuphatikizapo ntchito yomanga zipinda za sukulu. Chaka chatha tinatolera ndalama yoposa 60 percent pa ndalama imene tinayerekeza,” atero a Nyasulu.

Akuluakulu ena a khonsoloyi anaonjezerapo kuti ndalamazi ziwathandizira kumalizitsa ntchito yokonza misewu komanso kuonetsetsa kuti mzinda wa Mzuzu ndi wa ukhondo.

Mfumu Thula inatsimikiza kuti imema anthu kuti adzipereka ndalama za misonkho, zotchedwa City Rates.

Olemba: Lovemore Shaba

Related posts

Akubanja ayamikira boma powonesa chikondi mu nthawi ya zobvutayi

Mayeso Chikhadzula

ULADI MUSSA ATHOKOZA DR CHAKWERA

MBC Online

Govt commits to improve children’s welfare

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.