A Tsazo Thabwa a m’mudzi mwa Fayifi kwa mfumu yaikulu Dzoole B m’boma la Dowa akuti moyo wa pa banja lawo wasintha modabwitsa potsatira zokolora zochuluka zomwe anapeza atagwiritsa ntchito feteleza wa manyowa wa Mbeya.
Iwowa akuti anali mu umphawi wa dzaoneni, akhala akulandira mtukula pakhomo ndipo amadziwika bwino m’mudzi mwawo pochita maganyu kuti apeze thandizo la pabanja pawo.
Koma lero mkuluyu anatsekula golosale lomwe limakhala ndi katundu ochuluka komanso akuchita bizinesi yogula ndi kugulitsa mbewu, kuphatikiza ku ntchito za ulimi wa mbewu zosiyanasiyana.
Chitukukochi chinadza atalowa gulu losunga ndi kuchulukitsa ndalama la COMSIP mu cluster ya Kampanje ndipo iwo pamodzi ndi mamembala anzawo 48 anaphunzitsidwa kapangidwe ka fetelezayu.
“Nditaphunzira kupanga fetelezayu pogwiritsa ntchito feteleza monga wa Urea, phulusa, madeya ndi ndowe, ndinakolora chimanga, fodya ndi soya ochuluka ndipo zonse pamodzi nditagulitsa ndinapeza ndalama zokwana K3.5 million,” watero Thabwa.
Ndalamayi anagwiritsa ntchito kugula malo, kumanga nyumba ndi golosale ndipo akuti amapeza ndalama zosachepera K200,000 pa tsiku.