Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

NEEF yati sikupereka ndalama za ulere

Bungwe lobwereketsa ndalama la National Economic Empowerment Fund Limited (NEEF) lati sizoona kuti lasayina mgwirizano ndi mtsogoleri wa dziko lino kuti lidzipereka ku banja lililonse ndalama zokwana K50,000 zomwe sadzabweza.

Poyankhapo pa chikalata chomwe anthu ena akufalitsa pa masamba a mchezo, Ofalitsankhani ku bungwe la NEEF,  Elizabeth Mapemba, wati nkhaniyi ndi yabodza.

Mapemba wati anthu ena amaganizo oyipa ndi omwe akufalitsa bodzali pofuna kupomboneza a Malawi ponena kuti Presidential Grant 2024 ifikira mabanja onse m’dziko muno.

“NEEF imapereka ngongole motsata ndondomeko zoyikika bwino ndipo ngongole iliyonse imayenera kuti munthu abweze.

Komanso a Malawi adziwe kuti chilichose chomwe a NEEF amapanga komanso boma amachilengeza  kudzera mu njira zokhazikika monga pa wailesi zoulutsa mau,  zakanema komanso m’manyuzipepala,” watero Mapemba.

Iye wati akudziwa kuti  pali  akambelembele omwe akufuna kusocheretsa ndikubera a Malawi.

Related posts

‘Tigwiritse ntchito ndalama za mtukula pakhomo mwa nzeru’

Rabson Kondowe

Parliament passes two land-related bills

Romeo Umali

CS-EPWP hailed for improving livelihoods in Likoma

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.