Malawi Broadcasting Corporation
Local

CHITUKUKO CHIKUFIKA KONSEKONSE

Phungu wa kummawa kwa boma la Dowa a Richard Chimwendo  Banda omwenso ndi Nduna yazamaboma aang’ono ayamikira mtsogoleri wa dziko lino poonetsetsa kuti chitukuko chikufika m’madera onse a m’dziko muno.

A Chimwendo Banda ayankhula izi pomwe mtsogoleri wa dziko lino akuyembekezeka  kukaona momwe ntchito yomanga nyumba za asilikali a nkhondo zokwana 40  ku Mvera Support Battalion  mdera lawo ikuyendera.

A Chimwendo Banda ati Dr Chakwera akukwanitsa malonjezo awo ndipo ati nzosangalatsa kuti chitukuko ngati ichi chikuchitika mmadera onse a mdziko muno.

“M’mbuyomu nyumba zing’onozing’ono ndi zomwe amamanga zoti makolo akakhala ndi ana awiri atatu amadera nkhawa kuti anawa adzigona pati ena mpaka kumagona pa balaza koma taonani nyumbazi za maofisala   zokongola komanso nyumba za bwino kwambiri,” atero a Chimwendo Banda.

Iwo atinso dziko lino tsopano lanyamuka ndipo  zipatso zomwe  aMalawi akhala akuzifuna zibala mmagawo osiyanasiyana monga  chitukuko cha zomangamanga,  milatho komanso ku ulimi mwa zina.

Boma likumanga nyumba za asilikali zokwana 10000. Zina  mwa izo 4000  ndi za apolisi zina 4000 ndi za asilikali ankhondo ndipo nthambi za  asilikali a kundende komanso oona zotuluka komanso kulowa mdziko muno  alandira nyumba 1000 nthambi iliyonse.

Wolemba: Beatrice Mwape ndi McDonald Chiwayula.

#mbcmw
#mbcnews
#mbconlineservices

Related posts

Foundation bemoans red tape in development projects

MBC Online

Duwe helps Silver Strikers defeat Moyale

Romeo Umali

Nsanje DC pushes for irrigation farming

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.