Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

MFUMU CHIWERE YAYAMIKIRA BOMA POLIMBIKITSA CHITUKUKO

Mafumu ayamikira mtsogoleri wa dziko Dr Lazarus Chakwera  pantchito za chitukuko zomwe akuchita  mzigawo zonse za dziko lino.

Poyankhulapo m’boma la Dowa,  Senior Chief Chiwere,  yati kudzera mu utsogoleri wa Dr Chakwera,   dziko lino likhala ndi chitukuko chapamwamba. Izi ati ndi zomwe zikusintha miyoyo ya anthu ambiri.

Iwo athokozanso mtsogoleri wa dziko lino pokhala odzichepetsa ndi kumacheza ndi anthuwa.

Mfumuyi yapempha mtsogoleri  wa dziko lino kuti ntchito ya madzi akumwa ya Salima-Lilongwe Water Project itheke popeza ati anthu a mderali amavutika kuti apeze madzi  abwino akumwa.

Iwo apemphanso  boma kuti liwathandize kuti chimanga chidzipezeka mosavuta m’misika ya ADMARC.

Wolemba: Beatrice Mwape ndi McDonald Chiwayula.
#mbcmw

Related posts

PCL achieves 100% profit

Romeo Umali

Aphungu otsutsa akukana kukambirana za lamulo losintha kagulidwe ka mafuta agalimoto m’dziko muno

Rabson Kondowe

Religious leaders happy with Dr Chakwera’s development initiatives

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.