Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Chitukuko chifalikira m’boma lonse la Nsanje — Zikhale

Nduna ya za m’dziko, a Ken Zikhale Ng’oma, yalonjeza anthu ku Nsanje kuti boma lipitilira kukhazikitsa ntchito za chitukuko m’bomali ndi cholinga chotukula bizinesi zawo.

Poyankhula pa msonkhano wa chitukuko pa bwalo la Mpatsa CDSS mdera la pakati m’boma la Nsanje, a Zikhale Ng’oma, omwenso ndi mkulu okonza mapulani m’chipani cha MCP, ati ichi ndi chifukwa boma layika chidwi pobwezeretsa maulendo a njanji olumikiza bomali ndi maboma ena komanso dziko la Mozambique.

Pamsonkhanowo, a Ng’oma alandira anthu 300 ochoka ku chipani chotsutsa cha DPP kulowa MCP.

Related posts

‘Akabaza kalembetseni m’kaundula wa voti’

Romeo Umali

Zokonzekera gawo lachiwiri lokonza sikimu ya Mlambe zili mchimake

Romeo Umali

Apalasa kuchoka Lilongwe mpaka Blantyre pofuna kutolera K100 million

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.