Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Ndende zisintha – Boma

Nduna yoona zachitetezo cha m’dziko, a Ken Zikhale Ng’oma,  ati posachedwapa boma mogwirizana ndi dziko la China ligula zipangizo zomwe adziphunzitsira anthu amene ali ku ndende ntchito zosiyanasiyana zaluso lamanja.

Iwo adati izi zithandiza kuti akatuluka kundende adzitha kupeza zochita zowathandizira. Ndunayi yanena izi itayendera ndende ya Mzuzu.

Paulendowu zadziwikanso kuti ngakhale boma likupereka ndalama zachakudya kwa anthu amene ali ku ndende, sizikumafika msanga kaamba koti ma ofesi ena akuchedwetsa ndondomeko zina. Nkhaniyi siinasangalatse ndunayi yomwe inayimba phone pompo kuti vutoli likonzedwe.

Ndipo ndunayi yalamulanso kuti unduna wawo upereke galimoto ku ndende ya Mzuzu komwe bvuto la galimoto ndi lalikulu.

Pakadali pano, a Ng’oma apereka ndalama yokwana K1 million kuti ithandizire kumbali yachakudya pandendepo.

 

Olemba: Chisomo Manda

Related posts

‘Mtayakhasu ndi ulimi othana ndi njala’

Romeo Umali

Anthu 1.4 million alowa nkaundula wa zipangizo zaulimi zotsika mtengo

Rabson Kondowe

Launch of Tambala Cup this weekend

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.