Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Chikakula patuka, Ramadhan watumiza ‘leka’

Mphunzitsi wamkulu wa timu ya Mighty Mukuru Wanderers, Nsazurwimo Ramadhan, wati watula pansi udindowu kutsatira kugonja kwa timuyi mumasewero awiri motsatizana mu TNM Super League.

Ramadhan, yemwe adalonjeza kubweretsa chimwemwe kubanja la Manoma, waona ngati kumaloto atagonja ndi timu ya Mzuzu City Hammers ndi zigoli ziwiri kwa duu loweruka patangopita masiku ochepa timuyi itagonjaso ndi timu ya Silver Strikers ndi zigolinso ziwiri kwa duu.

Ramadhan, popereka kalata yotula pansi kwa mtsogoleri wa timuyi Thom Mpinganjira, wati sakufuna kukakamiza zinthu.

“Ngati tebulo silikufuna kukupatsa chakudya kulibwino kuzisiya,” iye watero.

Timu ya Wanderers ili ndi mapointi khumi ndi awiri pamndandanda wa matimu omwe akusewera mu ligi yaikuluyi ndipo ikusiyana ndi mapointi khumi ndi timu yomwe ikutsogola ya Silver Strikers ndipo onse asewera masewero okwana asanu ndi atatu.

Related posts

‘Pewani kufalitsa nkhani zabodza’

Romeo Umali

Achinyamata asamalire okalamba — Mayi Mbambande

Romeo Umali

Ana a m’mudzi bwerani muthandize kwanu – Mfumu Mwamulowe yatero

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.