Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News Nkhani Politics

DPP idanama — Kabwila

Ofalitsa nkhani ku chipani cha Malawi Congress (MCP), a Jessie Kabwila, ati chipani chotsutsa cha DPP chidanena bodza ku msonkhano wawo waukulu pamene adati m’dziko muno simukuchitika chitukuko pansi pa mtsogoleri wa dziko la Malawi, Dr Lazarus Chakwera.

A Kabwila amayankhula izi atayendera ntchito zachitukuko zomwe zili mu mzinda wa Blantyre.

Zina mwa ntchitozi ndi yomanga malo okwelera mabasi ku Mibawa, yomanga msewu ku Lunzu, msewu opita ku Machinjiri kuchoka msewu wa Magalasi, mlatho watsopano wa Makalanga ku Machinjiri ndi msewu olumikiza Makhetha ndi Ndirande.

Iwo anati ndi zokondweretsa kuona ntchito za chitukuko zikuperekanso mwayi wa ntchito kwa a Malawi.

A Kabwila aperekanso chitsanzo cha ntchito zobwezeretsa njanji ngati zina mwa zitukuko zomwe boma lidakhazikitsa.

Related posts

Flames drop three steps on FIFA rankings

Romeo Umali

MALAWI’S TOUGH FIGHT AGAINST WILDLIFE CRIMES BEARING FRUITS

MBC Online

Information dissemination key — MCCCI

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.