Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Politics

Chiganizo chotuluka mu mgwirizano tidzatsimikiza pa 19 July — UTM

Chipani cha UTM chalengeza ganizo lake lofuna kuchoka mu mgiwirizano wa Tonse Alliance.

Akuluakulu a chipanichi ndiwo anena izi lero kumsonkhano wa atolankhani umene achititsa munzinda wa Lilongwe.

Ena mwa akuluakulu amene ali pamsonkhanowo ndi mlembi wamkulu wa chipani chi, a Patricia Kaliati komanso mneneri wachipanichi, a Felix Njawala.

Mwazina, a Kaliati ati nkumano omwe anali nao umayenera kukhalapo potengera kuti chimwalireni mtsogoleri wa chipanichi Dr Saulos Chilima sanakhale nao.

Pazachilinganizo chotuluka mu mgwirizano wa Tonse, iwo ati ganizo lotsimikizika adzapereka pa nkumano wa pa 19 July mwezi uno.

Zipani zinanso zimene zili mu mgwirizanowu ndi monga People’s Party komanso MAFUNDE.

 

Related posts

Communities in Kasungu still shocked by ‘prophetic’ murders

Romeo Umali

Malawi Beach Soccer takes on Burundi

Romeo Umali

Ministry of Local Government calls for culture of cleanliness

McDonald Chiwayula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.