Malawi Broadcasting Corporation
Business Development Local Local News Nkhani

CADECOM ithandiza mabanja omwe akhudzidwa ndi njala ku Phalombe

Bungwe la mpingo wakatolika la Catholic Development Commission of Malawi (CADECOM) lapereka ndalama zokwana K63,150,000 ku mabanja 421 omwe akhudzidwa ndi njala kwa Mfumu yaikulu Phweremwe m’boma la Phalombe ndipo banja lililonse lalandira K150,000.

Mmodzi mwa akuluakulu a CADECOM, Vincent Tenthani, wati apereka ndalamazo kuti agule chakudya potsatira njala yomwe yadza kamba ka nyengo ya El nino komanso ngozi zachilengedwe zomwe zasokoneza ulimi m’bomalo.

A Tenthani ati apereka ndalamazo kwa anthu amene sangathe kugwira ntchito, kuphatikizapo okalamba ndi olumala.

Mmodzi mwa anthu omwe alandira nawo ndalamazo, mayi Andoleje Fulusa a zaka za mma 70, ayamikira bungweli ponena kuti tsopano akwanitsa kugula chimanga.

Ndithandizo lochokera ku bungwe la Trocaire, bungwe la CADECOM lati likufuna kufikira mabanja 891 ndi thandizo la ndalama m’bomalo.

 

Related posts

Iceland PM arrives for five-day visit

Rabson Kondowe

Ex-convicts arrested for suspected burglary

Romeo Umali

Good start for Moyale

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.