Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Atsiriza kufufuza za imfa ya anthu asanu ku Blantyre

A polisi ati katswiri opima matupi aanthu, Charles Dzamalala, watsiriza kupima matupi a anthu omwe  afa atamwa mowa wina kwa Manase ku Blantyre.

Mneneri wa apolisi mchigawo chakummwera, Joseph Sauka, wati zotsatirazi azitulutsa nthawi ina iliyonse.

A Sauka ati anthu asanuwa anamwalira mmodzi mmodzi atamwa mowawu, zomwe zinachititsa achipatala kuyamba ayimitsa kuti awiri mwa matupi a anthuwo asawaike mmanda kuti awapime kaye.

Anthu omwe anamwa mowawu, malinga ndi a Sauka, analipo asanu ndi atatu ndipo awiri ali mwakayakaya pomwe mmodzi akuwonetsa kusintha.

 

Related posts

MACODA launch disability act booklet

Romeo Umali

Mangochi residents petition Chakwera over rising water levels

Rabson Kondowe

Serve Malawians, Chakwera advises Mumba

Chisomo Manda
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.