Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Ayamba kumanga anthu ogulitsa “ambuye tengeni”

Apolisi mchigawo chakummwera ati tsopano ayamba kumanga anthu onse omwe akugulitsa mowa owopsa wa ‘ambuye tengeni’ omwe waphetsa anthu asanu kwa Manase ku Blantyre.

Anthu ena atatu ali m’chipatala.

Mneneri wa a polisi mchigawochi, a Joseph Sauka, ati apolisi ali kale mmadera osiyanasiyana komwenso akulanda mowawu, omwe ati ndi owopsa kwambiri.

“Cholinga chathu ndikuteteza anthu ku imfa zodza kamba kakumwa mowa osavomerezeka, omwenso ndi owopsa,” atero a Sauka.

Related posts

Catholic Church hailed as a partner in vocational education

Rabson Kondowe

‘Tithandizane potukula ntchito za umoyo’

Rabson Kondowe

Mother of seven receives aid from Lions Club following appeal

Alinafe Mlamba
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.