Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani

Chifukato cha a Chewa chithandiza mfumu Ngabu 

Bungwe la Malawi Chewa Heritage lapereka zipangizo zomangira nyumba ya mfumu yayikulu Ngabu m’boma la Nsanje.

Nyumba ya mfumuyi idaoonongeka ndi mphepo yamkhutho imene idawomba dera la Khuluvi m’mudzi wa Kaudzu.

Mtsogoleri wa bungwe la Chifukato Cha Achewa, Gogo Sosola, anati ndi kofunika kukhala mothandizana komanso modalirana panthawi yamavuto.

“Apapa tangoyamba ndipo tidzibwera bwera maka munthawi yamavuto komanso chisangalaro kuti tiyende limodzi ngati dziko,” Gogo Sosola anatero.

Mfumu yayikulu Ngabu anali okondwa polandira thandizoli.

“Ndine othokoza kwambiri pa zimene mwatipatsazi, ine ngati mfumu ndi makhala ku nyumba ya ufumu koma banja langa liri ndi pogwira,” iwo anatero.

Pamwambowu panali anthu osiyanasiya kuchokera ku boma, ochita malonda komanso mafumu, ndi ena ambiri.

Katundu amene anaperekedwa ndi monga malata komanso cement ndi ndalama.

Olemba: Stanley Kadzuwa

 

Related posts

Mtumbuka pleads with corporate world to support Netball

Romeo Umali

Wetlands, Wildlife, Rangers Day joint commemoration in Rumphi

Romeo Umali

President Chakwera visits Eastern Region

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.