Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

A Chakwera acheza ndi ochita malonda kunyumba ya boma

Mtsogoleri wa dziko lino, Dr. Lazarus Chakwera, masana ano akuyembekezeka kucheza ndi ochita malonda ochokera mmisika yosiyanasiyana ya  kuchigawo chakummawa kwa dziko lino.

Ochita malonda osachepera 300 ndiwo afika kunyumba ya boma ya Chikoko Bay ku Mangochi.

Mwazina, Dr. Chakwera akufuna kumva ena mwa mavuto amene anthuwa akukumana nawo komanso kupeza ena mwa mayankho a mavutowo.

Ena mwa ochita malondawa achokera ku misika ya ku Zomba, Machinga-Ntaja, Nsanama, Liwonde, Mangochi ndi misika ina.

 

Olemba: Mirriam Kaliza

Related posts

6 FAMILY MEMBERS DIE IN ROAD ACCIDENT

MBC Online

Mponda signs three year deal at Bullets

Romeo Umali

First Lady pledges support to childless women

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.