Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Msonkhano wa mabishop wa maiko atatu watha

Msonkhano wa bishop a maiko a Malawi, Zambia komanso Zimbabwe watha m’boma la Salima pomwe agwirizana zogwilira limodzi komanso kutumikira mokomera nkhosa zao maikowo pa ntchito yazaumoyo, maphunziro komanso zosamalira zachilengedwe.

Msonkhano-wu avomereza mfundo zoyendetsera gululi lomwe tsopano azilitcha kuti Association of Catholic Bishops in Zambia, Zimbabwe and Malawi.

Powerenga mfundozo, prezidenti wa mabishop M’Malawi muno Archbishop George Desmond Tambala ati mwa zina agwirizananso zoti likulu laguli likhale ku Lusaka mdziko la Zambia ndipo wapampando wake tsopano akhala mtsogoleri wa dziko la Zimbabwe.

Msonkhano wina ngati omwewu udzachitika mchaka cha 2027 mdziko la Zimbabwe.

Related posts

Chitipa Council approves K22 billion budget for 2025/2026

Romeo Umali

2 WIN BIG WITH BETIKA

Rabson Kondowe

MINISTRY OF TRADE FOR MORE DEVELOPMENT OF COOPERATIVES

McDonald Chiwayula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.