Malawi Broadcasting Corporation
Business Local Local News Nkhani

CRWB ipereka mphoto kwa makasitomala okhulupirika

Bungwe la Central Region Water Board (CRWB) lapereka mphoto kwa ena mwa makasitomala ake omwe amalipira madzi mokhulupirika.

Cholinga cha mphotozi ndi kufuna kulimbikitsa anthu ena, zimene akuti zikhoza kuthandiza kukweza ndi kupititsa patsogolo ntchito yogawa madzi chigawo chonse chapakati.

Ofalitsankhani ku CRWB, a Zephelino Mitumba, ndi amene ananena izi pa mwambowo umene umachitikira pa bwalo la masewero la Dowa Community m’boma la Dowa.

Iwo anati pali mavuto ambiri amene amakumananawo pa ntchito yopereka madzi, zimene zimachititsa kuti masiku ena madzi asamatuluke m’mipopi.

Makasitomala makumi atatu ndi amene alandira mphoto pa mwambowo.

 

Related posts

Pempho layankhidwa — Aphunzitsi okhudzidwa

Romeo Umali

Cool drop manufacturer moves to rectify product glitches

Alinafe Mlamba

Zintchito za Emmie Deebo zadodometsa eni kampani yasopo

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.