Malawi Broadcasting Corporation
Business Local Local News Nkhani

CRWB ipereka mphoto kwa makasitomala okhulupirika

Bungwe la Central Region Water Board (CRWB) lapereka mphoto kwa ena mwa makasitomala ake omwe amalipira madzi mokhulupirika.

Cholinga cha mphotozi ndi kufuna kulimbikitsa anthu ena, zimene akuti zikhoza kuthandiza kukweza ndi kupititsa patsogolo ntchito yogawa madzi chigawo chonse chapakati.

Ofalitsankhani ku CRWB, a Zephelino Mitumba, ndi amene ananena izi pa mwambowo umene umachitikira pa bwalo la masewero la Dowa Community m’boma la Dowa.

Iwo anati pali mavuto ambiri amene amakumananawo pa ntchito yopereka madzi, zimene zimachititsa kuti masiku ena madzi asamatuluke m’mipopi.

Makasitomala makumi atatu ndi amene alandira mphoto pa mwambowo.

 

Related posts

CSOs bang heads on Social Protection Programmes

Alinafe Mlamba

Creck appoints Kamwendo as head coach

MBC Online

Natural Resources Ministry needs K1.2 billion

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.