Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Sports Sports

SULOM yayankhulapo pa zomwe Mafco yachita

Bungwe loyang’anira masewero ampira muligi yaikulu ya mdziko muno la Super League of Malawi (SULOM) ladzudzula mchitidwe omwe timu ya Mafco yachita omwe ndi otsutsana ndi malamulo ampira.

Malinga ndi chikalata chomwe bungweli latulutsa zilango ziperekedwa mogwirizana ndi zomwe zachitika m’masewero apakati pa timu ya Nyasa Big Bullets ndi Mafco FC Lamulungu pa 6 October 2024.

Chikalatachi chasonyezanso kuti SULOM yawonera kanema yemwe akuwonetsa Wongani Lungu akupondedwa ndi osewera a timu ya Mafco zomwe ati n’zokhumudwitsa komanso n’zosaloledwa m’masewero ampira wamiyendo.

 

Related posts

Social Cash Transfer beneficiary turns cattle owner

Romeo Umali

G2G vessel arrives at Nacara Port with 22 Million litres of diesel for Malawi

Mayeso Chikhadzula

MALAWI COMMEMORATES INTERNATIONAL DAY OF EDUCATION

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.