Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Sports Sports

SULOM yayankhulapo pa zomwe Mafco yachita

Bungwe loyang’anira masewero ampira muligi yaikulu ya mdziko muno la Super League of Malawi (SULOM) ladzudzula mchitidwe omwe timu ya Mafco yachita omwe ndi otsutsana ndi malamulo ampira.

Malinga ndi chikalata chomwe bungweli latulutsa zilango ziperekedwa mogwirizana ndi zomwe zachitika m’masewero apakati pa timu ya Nyasa Big Bullets ndi Mafco FC Lamulungu pa 6 October 2024.

Chikalatachi chasonyezanso kuti SULOM yawonera kanema yemwe akuwonetsa Wongani Lungu akupondedwa ndi osewera a timu ya Mafco zomwe ati n’zokhumudwitsa komanso n’zosaloledwa m’masewero ampira wamiyendo.

 

Related posts

Evangelical Lutheran Church speaks on unity

Alinafe Mlamba

Parliament to promote the wellbeing of women, children and adolescents

Rabson Kondowe

Malawi’s infrastructural development promising

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.