Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Sports Sports

SULOM yayankhulapo pa zomwe Mafco yachita

Bungwe loyang’anira masewero ampira muligi yaikulu ya mdziko muno la Super League of Malawi (SULOM) ladzudzula mchitidwe omwe timu ya Mafco yachita omwe ndi otsutsana ndi malamulo ampira.

Malinga ndi chikalata chomwe bungweli latulutsa zilango ziperekedwa mogwirizana ndi zomwe zachitika m’masewero apakati pa timu ya Nyasa Big Bullets ndi Mafco FC Lamulungu pa 6 October 2024.

Chikalatachi chasonyezanso kuti SULOM yawonera kanema yemwe akuwonetsa Wongani Lungu akupondedwa ndi osewera a timu ya Mafco zomwe ati n’zokhumudwitsa komanso n’zosaloledwa m’masewero ampira wamiyendo.

 

Related posts

Super League teams to honour Chilima during match week 10

Alinafe Mlamba

Othamanga akufuna kuthandiza ntchito za umoyo kudzera m’masewero

Alinafe Mlamba

Experts should guide on crop alternatives –Meteorologist

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.