Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Sports Sports

SULOM yayankhulapo pa zomwe Mafco yachita

Bungwe loyang’anira masewero ampira muligi yaikulu ya mdziko muno la Super League of Malawi (SULOM) ladzudzula mchitidwe omwe timu ya Mafco yachita omwe ndi otsutsana ndi malamulo ampira.

Malinga ndi chikalata chomwe bungweli latulutsa zilango ziperekedwa mogwirizana ndi zomwe zachitika m’masewero apakati pa timu ya Nyasa Big Bullets ndi Mafco FC Lamulungu pa 6 October 2024.

Chikalatachi chasonyezanso kuti SULOM yawonera kanema yemwe akuwonetsa Wongani Lungu akupondedwa ndi osewera a timu ya Mafco zomwe ati n’zokhumudwitsa komanso n’zosaloledwa m’masewero ampira wamiyendo.

 

Related posts

Abwenzi a Boma pachitukuko alonjeza thandizo pantchito zachuma

Rabson Kondowe

Malawi gets K1.7bn from AfDB

Yamikani Simtowe

MCP North-North Region has new Deputy Regional Chairperson

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.