Malawi Broadcasting Corporation
Development Local News Nkhani

Ndine otetezedwa tsopano, watero mnyamata waku Salima

Mnyamata wochokera dera lamfumu yaikulu Mwanza m’boma la Salima, Chinsinsi Luka, yemwe ndi alubino, tsopano wati ndiwosangalala kamba kanyumba yomwe boma lamumangira.

Nyumbayi ndimbali imodzi ya ntchito yomanga nyumba kwa anthu achi alubino yomwe mtsogoleri wadziko lino anaikhazikitsa.

Unduna wa zamalo komanso unduna owona kuti pasamakhale kusiyana pakati pamayi ndi abambo apereka nyumbayi kwanyamatayu ndi banja lake lero.

Nduna yoona kuti pasamakhale kusiyana pakati pa amayi ndi abambo, a Jean Sendeza, alimbikitsa anthu m’dziko muno kuteteza anthu achi alubino.

Ndipo nduna ya zamalo, a Deus Gumba, ayamikira ntchito yamtunduwu, kunena kuti ndichitsimikizo kuti boma limaganizira umoyo wa aliyense m’dziko muno.

Pakali pano, boma lamanga nyumba za anthu achi alubino m’dziko muno zokwana 65.

 

Related posts

Former DPP leaders in the north join PDP

Rabson Kondowe

Region 5 enhances global partnerships

Romeo Umali

Sparc sponsors BAM’s AGM

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.