Malawi Broadcasting Corporation
Crime Development Local Local News Nkhani

Nzika ya Niger akuyisunga ku Maula

Nzika ya ku Niger, a Osman Muhammad, akuyisunga ku ndende ya Maula khoti litakana pempho lake la belo.

Lachitatu masana, Muhammad anakaonekera kubwalo la Magistrate la Mkukula ku Lumbadzi pa mlandu opezeka ndi mankhwala oopsya amene ali ozunguza ubongo komanso ofuna kuzembetsa mankhwalawa kudzera m’dziko muno.

Malinga ndi ofalitsankhani wa Polisi ya KIA, a Sapulain Chitonde Lee, mlanduwu ukhala ukupitilira Lachisanu pa 10 May pa bwalo lomweli.

A Muhammad adawapeza ndi mankhwala oopsya komanso ozunguza bongo pa bwalo la ndege la KIA pamene amafuna kuti pite m’dziko la Germany.

Iwo adawapeza ndi mankhwala otchedwa Diamorphine okwana 51 omwe adawabisa mu zikwama zawo ndi ena okwana 13 amene anali kumalo okhalira.

#MBCDigital
#Manthu

Related posts

‎Relegated Hammers turn pain into power in Castel Cup run

MBC Online

Cost of housing is expensive in BT, MZ — CFSC

Romeo Umali

Chakwera for co-existence, rallies youths on development

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.