Malawi Broadcasting Corporation
Crime Development Local Local News Nkhani

Nzika ya Niger akuyisunga ku Maula

Nzika ya ku Niger, a Osman Muhammad, akuyisunga ku ndende ya Maula khoti litakana pempho lake la belo.

Lachitatu masana, Muhammad anakaonekera kubwalo la Magistrate la Mkukula ku Lumbadzi pa mlandu opezeka ndi mankhwala oopsya amene ali ozunguza ubongo komanso ofuna kuzembetsa mankhwalawa kudzera m’dziko muno.

Malinga ndi ofalitsankhani wa Polisi ya KIA, a Sapulain Chitonde Lee, mlanduwu ukhala ukupitilira Lachisanu pa 10 May pa bwalo lomweli.

A Muhammad adawapeza ndi mankhwala oopsya komanso ozunguza bongo pa bwalo la ndege la KIA pamene amafuna kuti pite m’dziko la Germany.

Iwo adawapeza ndi mankhwala otchedwa Diamorphine okwana 51 omwe adawabisa mu zikwama zawo ndi ena okwana 13 amene anali kumalo okhalira.

#MBCDigital
#Manthu

Related posts

GOVT PLEDGES TO SUPPORT CREATIVE INDUSTRY

MBC Online

MANEPO yayamikira Madam Chakwera polimbana ndi nkhanza za anthu achikulire

Alinafe Mlamba

Kukhala madyelero pomwe asilamu akukondwelera Eid

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.