Malawi Broadcasting Corporation
Business Development Local News Nkhani

Titukuka tikakonza misonkho, magetsi — Old Mutual

Mkulu wa kampani ya Old Mutual m’dziko muno, a Edith Jiya, ati dziko lino likuyenereka kuti likonze mavuto a magetsi komanso misonkho pofuna kuti dzikoli litukuke kudzera mu ndondomeko ya ATM.

Ndondomekoyi anakhazikitsa ndi mtsogoleri wa dziko lino Dr Lazarus Chakwera, mu mwezi wa February, ndipo cholinga chake ndi kukweza chuma cha dziko lino pogwiritsa ntchito ulimi, zokopa alendo komanso migodi.

A Jiya amayankhula izi pa mwambo wa akuluakulu a kampane zambiri m’boma la Mangochi komwe anati mfundozi zitha kutukula dziko la Malawi mwa ka nthawi kochepa.

Uthenga wawo pa mwambowu, iwo anati anthu akufunika kuti adziwe zakufunika kopanga katundu woti azigwiritsidwa ntchito m’dziko muno m’malo moyitanitsa kunja kwa dziko lino.

 

Related posts

Chileka Police condemns suicide

Rabson Kondowe

Chakwera appoints ministerial committee for VP state funeral

Romeo Umali

Police arrest two for alleged possession of medical drugs

Mayeso Chikhadzula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.