Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

‘Malo nawa koma tionepo chitukuko pasanathe zaka ziwiri’

Mwambo opereka malo kwa atsikana osewera mpira wa miyendo mutimu ya Scorchers wayamba ndi kupereka zikalata zaumwini kwa osewerawa ku unduna wa zamalo ku Lilongwe, komwe atsikanawa asonkhana limodzi ndi aphunzitsi awo.

Malinga ndi chikalata chomwe unduna wazamalo wawerenga pamwambowu, atsikanawa akuyembekezeka kupanga chitukuko pamalowa pasanadutse zaka ziwiri ndikuti akalephera kutero, boma lidzatenganso malowa.

Pamwambowu pali akuluakulu a ku unduna wa za malo, unduna wa zamasewero komanso akuluakulu a bungwe loyendetsa mpira wa miyendo m’dziko muno la Football Association of Malawi ndipo mlendo olemekezeka ndi Chikumbutso Mtumodzi, mlembi wamkulu oyang’anira ntchito zosiyanasiyana ku unduna wa zamasewero.

Related posts

Lucius anali katswiri, watero ‘Reggae Ambassador’ Charles Sinetre

Romeo Umali

Chitetezo munthawi ya chisankho ndi chofunika

Romeo Umali

‘Pewani m’chitidwe ogwiritsa ntchito ana’

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.