Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

‘Tidziyamba ndife aMalawi kutsatsa malonda a dziko lathu’

Mtsogoleri wadziko lino, Dr Lazarus Chakwera, wati dziko lino silikuchita bwino kwenikweni chifukwa choti timataya nthawi ndikufalitsa zinthu zoononga mbiri yathu m’malo mofalitsa zambiri zabwino zomwe zikuchitika m’dziko muno.

Dr Chakwera ati tidziyamba ndife aMalawi kuonetsera zinthu zabwino zimene zili m’dziko muno.

Iwo ayankhula izi pamwambo wotsegulira sabata ya msonkhano waulimi, zokopa alendo komanso migodi omwe ukuchitikira ku Bingu International Convention Centre mumzinda wa Lilongwe.

Dr Chakwera atsindika kufunika kolimbikira zokhazo zopindulitsa dziko monga ulimi wamakono, ntchito zamigodi komanso zokopa alendo.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

TCM yachenjeza aphunzitsi osapezeka m’kaundula wawo

Beatrice Mwape

Adzudzula zipani zomwe zikufuna kuti MEC isagwiritse chiphaso cha unzika pazisankho

MBC Online

SINDIKUONA TSOGOLO KU CHIPANI CHA DPP – CHAMBO

Mayeso Chikhadzula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.