Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

‘Malo nawa koma tionepo chitukuko pasanathe zaka ziwiri’

Mwambo opereka malo kwa atsikana osewera mpira wa miyendo mutimu ya Scorchers wayamba ndi kupereka zikalata zaumwini kwa osewerawa ku unduna wa zamalo ku Lilongwe, komwe atsikanawa asonkhana limodzi ndi aphunzitsi awo.

Malinga ndi chikalata chomwe unduna wazamalo wawerenga pamwambowu, atsikanawa akuyembekezeka kupanga chitukuko pamalowa pasanadutse zaka ziwiri ndikuti akalephera kutero, boma lidzatenganso malowa.

Pamwambowu pali akuluakulu a ku unduna wa za malo, unduna wa zamasewero komanso akuluakulu a bungwe loyendetsa mpira wa miyendo m’dziko muno la Football Association of Malawi ndipo mlendo olemekezeka ndi Chikumbutso Mtumodzi, mlembi wamkulu oyang’anira ntchito zosiyanasiyana ku unduna wa zamasewero.

Related posts

Ufa othandizira ovutika ndi njala wafika

Blessings Kanache

Mbali ina ya msewu wa Chiwembe sanamange bwino — Chimwendo Banda

Romeo Umali

‘Timanga wina aliyense oyambitsa ziwawa zandale’

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.