Malawi Broadcasting Corporation
Health Local Local News Nkhani

Mudzafufuze abale anu — Zomba Mental

Chipatala cha Zomba Mental chati chili ndi anthu 27 amene anamaliza kulandira thandizo la mankhwala koma amakanika kuti atuluke chifukwa abale awo amawakana.

A Harry Kawiya, ofalitsankhani wa chipatalachi, ndiwo amanena izi pamene amayendera malowa pamodzi ndi olembankhani kuti aone m’mene iwo akugwilira ntchito.

A Kawiya adalangiza anthu amene abale awo anasowa pakale kuti akafufuze ku chipatalachi chifukwa ena mwa iwo akhala pa malowa kwa zaka zokwana khumi.

“Tili ndi ena omwe kwawo sitimakudziwa mpakana tinapereka maina malinga ndi madera omwe anachokera,” iwo anatero.

Mwa anthu 27 amene ali ku Zomba Mental, 17 ndi abambo ndipo khumi ndi amayi.

Chipatala cha malingaliro amuubongo cha Zomba chili ndi chiwerengero cha odwala choposa 400.

#MBCDigital
#Manthu

Related posts

Malawi gears up for 2024 IDPD

McDonald Chiwayula

200 THOUSAND HOUSEHOLDS TO ACCESS ELECTRICITY UNDER MEAP PROJECT

MBC Online

‘Stay strong’: Breast cancer survivor finds hope and support

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.