Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Nkhalango zikupitilira kusakazidwa

Unduna owona za chilengedwe ndi kusintha kwa nyengo wati ndiokhumudwa ndimomwe anthu akupitilizira kuononga nkhalango m’dziko muno.

Mmodzi wa akuluakulu ku undunawu, a Titus Zulu, ndiwo ayankhula izi ku Lusangazi m’chigawo chakumpoto pamene amapereka zipangizo zotetezera nkhalango kwa anthu amene amakhala m’midzi yozungulira nkhalango ya Viphya.

A Zulu ati ndizomvetsa chisoni kuti nkhalango zikupitilira kutha, zomwe zikuonjezera mavuto a kusintha kwanyengo m’dziko muno.

“Kuononga nkhalango ndikudzipweteka tokha chifukwa munkhalangoyi mumapezeka zinthu zambiri zotithandiza ife tomwe ngati anthu,” anatero a Zulu.

A Steven Kalanga a ku Lusangazi kulandira zipangizo

Iwo anati kuononga nkhalango kukupangitsa kuti mvula isamabwere mokhulupirika komanso kuti mitsinje idziphwa, zomwe anati zikusokoneza chikonzero cholimbikitsa ulimi wamthilira.

A Zulu anati poona kuti antchito oteteza nkhalango akuchepa, unduna wawo waganiza zogwilira ntchito yoteteza nkhalangozi ndi anthu okhala mozungulira nkhalangozi.

Wolemba: Henry Haukeya

Related posts

Mabedi wavomereza kuti Flames ili mu gulu lovuta mu AFCON 2025

MBC Online

A Chakwera ndagoma nawo — Mwambande

Romeo Umali

CADECOM ithandiza mabanja omwe akhudzidwa ndi njala ku Phalombe

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.