Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Politics

A Chakwera ndagoma nawo — Mwambande

Phungu wadera la kumpoto m’boma la Karonga, a Mungasulwa Mwambande, wati chimene chachititsa kuti alowe chipani cha Malawi Congress (MCP) ndi zitukuko zimene President Dr Lazarus Chakwera akumwaza m’dziko muno mosayang’ana dera kapena zigawo.

A Mwambande, amene amayankhula ku Iponga pa msonkhano wandale powalandira m’chipanichi, ati anthu ochuluka mdera lawo ndi okondwa ndi utsogoleri umene ulipo pano, moti akufuna upitilire mpakana 2030 kuti dziko lino likhale losinthika.

Iwo anali a chipani cha Democratic Progressive ndipo anakhalapo wachiwiri kwa nduna yoona za migodi.

Mlembi wa chipani cha MCP, a Richard Chimwendo Banda, yemwe anali mlendo wolemekezeka pa mwambowu, anamema anthu kuti akhale pambuyo pa Dr Chakwera, omwe cholinga chawo ndi kusintha miyoyo ya anthu onse m’dziko muno.

Olemba: Musase Cheyo
Ojambula: Boston Tembo

Related posts

Mtukula Pakhomo beneficiaries set to increase in Mzimba

Romeo Umali

SOCIAL CASH TRANSFER PROGRAMME SUPPORTS 1.4 MILLION INDIVIDUALS

McDonald Chiwayula

David versus Goliath affair in Airtel Top 8’s eighth season opener

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.