Malawi Broadcasting Corporation
News Nkhani

Bushiri apereka chakudya kwa ovutika ku Mangochi

Pamene anthu ena  akupitilira kusautsika ndi vuto la njala m’boma la Mangochi, Mneneri Shepherd Bushiri wapeleka chimanga kwa anthu amene amakhala pafupi  ndi Goshen city ku dera la mfumu yaikulu Nankumba.

Mayi Dolasi Baluti anauza MBC kuti Ng’amba yawavuta kwabasi ndipo sakuyembekeza kuti akolora kanthu.

Iwo nathokoza a Bushiri  chifukwa cha thandizoli.

Poyankhula pa sukulu ya pulaimale ya Namazizi, a Bushiri anati ndikofunika kuthandizana wina ndi mnzake zinthu zikavuta.

Mneneri wa mpingo wa ECG-Jesus Nation yu anapemphanso   kampani ndi mabungwe akufuna kwabwino kuti athandize boma popereka chakudya kwa anthu.

“Inde njala yavuta, koma n’nafuna tigawane nawo anthu amene akukhala moyandikana ndi Goshen  City kuti nawonso  apeze chakudya.Ine sindingakwanitse kufikira aliyense, ndichifukwa chake tikuyenera kugwirana manja, “anatero a Bushiri.

Olemba Mirriam Kaliza.

Related posts

Tithandizeni kuthana ndi ngongole – Mzuzu City Council

Rabson Kondowe

Bambo alamulidwa agwire jere kwa zaka 12 atagwilira

Romeo Umali

Malawi calls for strengthened collaboration in the utilisation of the Central Corridor

Mayeso Chikhadzula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.