Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Zokonzekera za Misa yapadera yokumbukira malemu Dr Chilima zili mkati

Olemba: Timothy Kateta

Zokonzekera za mwambo wa misa yapadera yokumbukira yemwe adali wachiwiri kwa mtsogoleri wadziko lino, malemu Dr Saulos Chilima, zili mkati ku Nsipe m’boma la Ntcheu.

Mapempherowa akuyembekezeka kuchitika loweruka lino pa 20 July.

Mwambo wa Misayi uchitika patatha masiku 40 chichitikireni ngozi ya Ndege imene idapha malemu Chilima ndi anthu ena asanu ndi atatu mu nkhalango ya Chikangawa pa 10 June chaka chino.

Wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino, Dr Michael Usi, akuyembekezeka kukakhala nawo pamwambo wamapempherowu, umene udzachitikire pa bwalo la Nsipe Catholic, pafupi ndi manda amene kudaikidwa malemu Chilima.

Enanso womwe akuyembekezeka kudzakhala nawo ku mwambowu ndi Inkosi ya Makhosi Gomani yachisanu, akuluakulu aboma ndi mafumu.

Bishop Peter Adrian Chifukwa wa Dedza Diocese ndi yemwe adzatsogolere mapempherowa.

Related posts

CTS Courier yati ikufuna kupereka mwayi watchito kwa achinyamata

Rabson Kondowe

Chakwera to promote trade in Nkhata Bay 

Romeo Umali

Greenbelt yagulitsa matumba opyola 3,000 ku NFRA

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.