Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Zokonzekera za Misa yapadera yokumbukira malemu Dr Chilima zili mkati

Olemba: Timothy Kateta

Zokonzekera za mwambo wa misa yapadera yokumbukira yemwe adali wachiwiri kwa mtsogoleri wadziko lino, malemu Dr Saulos Chilima, zili mkati ku Nsipe m’boma la Ntcheu.

Mapempherowa akuyembekezeka kuchitika loweruka lino pa 20 July.

Mwambo wa Misayi uchitika patatha masiku 40 chichitikireni ngozi ya Ndege imene idapha malemu Chilima ndi anthu ena asanu ndi atatu mu nkhalango ya Chikangawa pa 10 June chaka chino.

Wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino, Dr Michael Usi, akuyembekezeka kukakhala nawo pamwambo wamapempherowu, umene udzachitikire pa bwalo la Nsipe Catholic, pafupi ndi manda amene kudaikidwa malemu Chilima.

Enanso womwe akuyembekezeka kudzakhala nawo ku mwambowu ndi Inkosi ya Makhosi Gomani yachisanu, akuluakulu aboma ndi mafumu.

Bishop Peter Adrian Chifukwa wa Dedza Diocese ndi yemwe adzatsogolere mapempherowa.

Related posts

Wakabaza waphula K200 million ya BetPawa

Romeo Umali

‘Mgwirizano ndi ofunika pa ntchito yobwezeretsa chilengedwe’

Rabson Kondowe

Ntchito ndi zambiri ku Israel koma tikufuna olimbika, latero boma la Israel

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.