Malawi Broadcasting Corporation
Development Entertainment Local Music News

Zikomo Ambuye — Avokado

Oyimba nyimbo za chamba cha Amapiano, Christopher ‘Avokado’ Malera wayamika Mulungu pomupulumutsa pa ngozi ya galimoto yomwe idachitika Lachiwiri m’mawa ku Mvera m’boma la Dowa.

Asadachite ngozi

Galimoto lake linawombana ndi wa njinga yamoto yemwe akuti amayenda mbali yake.

Atachita ngozi

Koma Avokado wati sanavulale paliponse kupatulapo wanjingayo, amene wavulala mwendo ndipo akulandira thandizo pa chipatala chachikulu cha m’bomalo.

Galimotolo lidatembenuzika katatu

“Ubwino wake ndinamanga lamba wa galimoto langa lomwe linatembenuzika katatu,” iye anatero.

Katswiri oyimbayu posachedwapa adatulutsa nyimbo yotchedwa ‘Msandipitilire Yesu’.

 

Related posts

Chakwera hails global efforts to boost electricity access in Africa

Mayeso Chikhadzula

Chief Kasumbu re-instated

Romeo Umali

First Lady calls for more financing of women empowerment programmes

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.