Malawi Broadcasting Corporation
Development Entertainment Local Music News

Zikomo Ambuye — Avokado

Oyimba nyimbo za chamba cha Amapiano, Christopher ‘Avokado’ Malera wayamika Mulungu pomupulumutsa pa ngozi ya galimoto yomwe idachitika Lachiwiri m’mawa ku Mvera m’boma la Dowa.

Asadachite ngozi

Galimoto lake linawombana ndi wa njinga yamoto yemwe akuti amayenda mbali yake.

Atachita ngozi

Koma Avokado wati sanavulale paliponse kupatulapo wanjingayo, amene wavulala mwendo ndipo akulandira thandizo pa chipatala chachikulu cha m’bomalo.

Galimotolo lidatembenuzika katatu

“Ubwino wake ndinamanga lamba wa galimoto langa lomwe linatembenuzika katatu,” iye anatero.

Katswiri oyimbayu posachedwapa adatulutsa nyimbo yotchedwa ‘Msandipitilire Yesu’.

 

Related posts

Don’t politicise distribution of relief items-DODMA

Alinafe Mlamba

FIRST LADY HAILS MUSLIM WORLD LEAGUE FOR PUMPING K8.5 BN FOR ORPHANS’ EDUCATION SUPPORT

MBC Online

Chilli farming offers economic lifeline for smallholder farmers

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.