Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Wobera anthu m’magalimoto amugamula zaka zitatu kundende

Bwalo la milandu la First Grade Magistrate ku Karonga lagamula a Mussa Banda kuti akakhale kundende kwazaka zitatu ndikugwira ntchito yakalavula gaga chifukwa chopezeka olakwa pamilandu iwiri yobera anthu mumagalimoto.

Bwaloli, kudzera kwa oyimira boma pamilandu, a George Manda linamva kuti a Banda pa 10 August chaka chino, ananyamula a Keshton Matandala mugalimoto yawo ya Honda Fit pa Tobi m’msewu wa M1 pomwe amapita ku Rumphi kukagula mtedza.

Patangodutsa nthawi pang’ono, galimotoyo inayima ndipo oyendetsa anati sapitilira ndi ulendowu.

Atamva izi, a Mwatandala anafuna kutsika ndipo anayesetsa kutsegula chitseko koma anaona kuti chinali chotseka.

Kenaka bwaloli linamva kuti m’modzi mwa anthu amene anali nawo mugalimoto  anayesa kuwathandizira kutsegula chitseko ndipo zinatheka.

Atatsika, a Matandala anazindikira kuti ndalama zawo zokwana K1.7 million zikusowa muchikwama chawo.

Malinga ndi a Banda pofotokezera bwaloli, izi zinachitikiranso a Kondwani Mwanganda omwe anaberedwanso K2 million pa 11 August 2024 pomwe amapita ku Rumphi  kukagulanso mteza.

Related posts

Lucius anali bwenzi lama Rasta — Ras Jonah

Romeo Umali

Kaneneni ku Polisi anthu akakulakwirani pa Intaneti — MACRA

Romeo Umali

Southern Africa’s Baptist women encouraged to live purposefully

McDonald Chiwayula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.