Malawi Broadcasting Corporation
News Nkhani

Tiyeni tilange ana moyenera —Bushiri

Mneneri wa mpingo wa Enlightened Christian Gathering (ECG), Shepherd Bushiri, wadzudzula mchitidwe olanga ana mopitilira muyeso akalakwitsa, ponena kuti izi ndi nkhanza.

Iwo anena izi pamene amagulira katundu osiyanasiyana mwana  wa mmudzi mwa Mndola, Mfumu yaikulu Kambwiri m’boma la Salima, amene anadyetsedwa dowe wamuwisi ochuluka masiku apitawa atagwidwa akuba m’munda.

Mneneriyu wati nkhani ya mwanayu ndiyomvetsa chisoni ndipo walonjeza kuti amuthandiza kuti achite maphunziro ake ndikudzakhala mzika yodalirika.

Katundu yemwe amugulirayu ndikuphatikizapo zovala,nsapato komanso zofunda.

Anthu osiyanasiyana, kuphatizikapo bungwe la Malawi Human Rights Commission, adzudzula amene anachitira nkhanza mwanayu ndipo apempha boma kuti lilowelerepo.

Related posts

Illovo ithandiza okhudzidwa ndi kusefukira kwa madzi ku Nkhotakota

Romeo Umali

Kalindo back in court for the firearm acquisition case

Rabson Kondowe

Malawi launches first early-maturing pigeonpea variety

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.