Malawi Broadcasting Corporation
News Nkhani

Tiyeni tilange ana moyenera —Bushiri

Mneneri wa mpingo wa Enlightened Christian Gathering (ECG), Shepherd Bushiri, wadzudzula mchitidwe olanga ana mopitilira muyeso akalakwitsa, ponena kuti izi ndi nkhanza.

Iwo anena izi pamene amagulira katundu osiyanasiyana mwana  wa mmudzi mwa Mndola, Mfumu yaikulu Kambwiri m’boma la Salima, amene anadyetsedwa dowe wamuwisi ochuluka masiku apitawa atagwidwa akuba m’munda.

Mneneriyu wati nkhani ya mwanayu ndiyomvetsa chisoni ndipo walonjeza kuti amuthandiza kuti achite maphunziro ake ndikudzakhala mzika yodalirika.

Katundu yemwe amugulirayu ndikuphatikizapo zovala,nsapato komanso zofunda.

Anthu osiyanasiyana, kuphatizikapo bungwe la Malawi Human Rights Commission, adzudzula amene anachitira nkhanza mwanayu ndipo apempha boma kuti lilowelerepo.

Related posts

Chakwera akhala nawo pa Misa ya mayi Shanil Dzimbiri

MBC Online

Macra’s muuni fund empowers innovators

Romeo Umali

‘We are suffering’: Villagers in Lilongwe demand action over pollution

Yamikani Simtowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.