Malawi Broadcasting Corporation
News Nkhani

Tiyeni tilange ana moyenera —Bushiri

Mneneri wa mpingo wa Enlightened Christian Gathering (ECG), Shepherd Bushiri, wadzudzula mchitidwe olanga ana mopitilira muyeso akalakwitsa, ponena kuti izi ndi nkhanza.

Iwo anena izi pamene amagulira katundu osiyanasiyana mwana  wa mmudzi mwa Mndola, Mfumu yaikulu Kambwiri m’boma la Salima, amene anadyetsedwa dowe wamuwisi ochuluka masiku apitawa atagwidwa akuba m’munda.

Mneneriyu wati nkhani ya mwanayu ndiyomvetsa chisoni ndipo walonjeza kuti amuthandiza kuti achite maphunziro ake ndikudzakhala mzika yodalirika.

Katundu yemwe amugulirayu ndikuphatikizapo zovala,nsapato komanso zofunda.

Anthu osiyanasiyana, kuphatizikapo bungwe la Malawi Human Rights Commission, adzudzula amene anachitira nkhanza mwanayu ndipo apempha boma kuti lilowelerepo.

Related posts

All set for the enthronement of Bishop Mchombo of the Anglican Church

Rabson Kondowe

Mulanje Peaks and Rhythms Festival set for this month end

Romeo Umali

Jah Prahzah, Onesimus to tussle for Artist of the Year

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.