Malawi Broadcasting Corporation
News Nkhani

Tiyeni tilange ana moyenera —Bushiri

Mneneri wa mpingo wa Enlightened Christian Gathering (ECG), Shepherd Bushiri, wadzudzula mchitidwe olanga ana mopitilira muyeso akalakwitsa, ponena kuti izi ndi nkhanza.

Iwo anena izi pamene amagulira katundu osiyanasiyana mwana  wa mmudzi mwa Mndola, Mfumu yaikulu Kambwiri m’boma la Salima, amene anadyetsedwa dowe wamuwisi ochuluka masiku apitawa atagwidwa akuba m’munda.

Mneneriyu wati nkhani ya mwanayu ndiyomvetsa chisoni ndipo walonjeza kuti amuthandiza kuti achite maphunziro ake ndikudzakhala mzika yodalirika.

Katundu yemwe amugulirayu ndikuphatikizapo zovala,nsapato komanso zofunda.

Anthu osiyanasiyana, kuphatizikapo bungwe la Malawi Human Rights Commission, adzudzula amene anachitira nkhanza mwanayu ndipo apempha boma kuti lilowelerepo.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Kamang’aleni akakuchitirani nkhanza — Mfumu Mwamlowe

Rudovicko Nyirenda

Apolisi agwira akuba amenenso anagwililira ophunzira ku Domasi Institute College

Charles Pensulo

US imposes travel ban on Malawi officials over corruption allegations

Alinafe Mlamba
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.