Malawi Broadcasting Corporation
News Nkhani

Adzudzula aphungu kamba kosapereka ulemu kwa Sipikala

Mmodzi mwa akuluakulu a chipani cha MCP ku nyumba ya malamulo,  a Ulemu Chilapondwa, adzudzula aphungu anyumba ya malamulo kamba ka khalidwe losapereka ulemu kwa Sipikala wa nyumba ya malamulo a Catherine Gotani Hara.

A chilapondwa, omwe ndi phungu wadera la Ntchisi South, anadandaula kuti atatulutsidwa mnyumbayi lachitatu sabata yatha, phungu wadera la Rumphi East, a Kamlepo Kalua, anakalankhula mawu onyoza sipika wanyumbayi pa masamba amchezo.

Poyankhapo pankhaniyi, mtsogoleri wazokambirana mnyumba ya malamulo, a Richard Chimwendo Banda, adandaula komanso kudzudzula  khalidwe limene adadonyeza a Kalua, yemwe akuti adanyoza mayi Catherine Gotani Hara polankhula ndi atolankhani sabata yatha.

Wachiwiri kwa sipika wanyumba yamalamulo, a Madalitso Kazombo, anatsindika kufunika kopeleka ulemu kwa mtsogoleri wanyumbayi yemwe ndi sipikala, ponena kuti malamulo a nyumbayi amafotokoza momveka bwino pa nkhani ya ulemu kwa atsogoleri.

Related posts

World Vision seeks partnership in ECD

Mayeso Chikhadzula

President Chakwera ikakisye ikomiti ya makambala ga boma iyakwendesya ifwa ya Chilima

Romeo Umali

Chitipa gears up for Misuku motorbike racing

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.