Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Titukule sukulu za mkombaphala – Joe Ching’ani

Yemwe akufuna kudzayimira  chipani cha Malawi Congress (MCP) pampando wa phungu kum’mwera  m’boma la Ntcheu, a Joe Ching’ani, ati pakufunika kulimbikitsa maphunziro a sukulu za mkombaphala ngati njira imodzi yotukula maphunziro m’dziko muno.

Iwo amayankhula izi m’boma la Ntcheu pomwe amatsekulira sukulu ya mkombaphala ya Mwanang’ombe, yomwe ayimanga ndi ndalama pafupipafupi K7 miliyoni m’dera la mfumu yayikulu Phambala m’bomali.

Iwo ati akadzasankhidwa kukhala phungu waderali,  adzapitiriza kupereka zitukuko zosiyanasiyana  potsata  mfundo za masomphenya a dziko lino a Malawi 2063, omwe mtsogoleri wa dziko lino Dr  Lazarus Chakwera  akulimbikitsa.

M’mawu ake, mfumu yayikulu Inkosi Phambala yati zomwe a Ching’ani apanga ndi zinthu zapamwamba.

 

Olemba: Thoccoh Jumpha

Related posts

Outbreak kills dogs in Blantyre

Rabson Kondowe

Cultural festivals are crucial for tourism — Mzuzu City Council

Romeo Umali

Government is creating jobs – Chimwendo Banda

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.