Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News

Titsegula misewu-yi pofika December chaka chino — Hara

 

Nduna ya zamtengatenga a Jacob Hara ati pofika December misewu ya Kenyatta komanso Mzimba yomwe akuikonza mu mzinda wa Lilongwe itsegulidwa.

Ndunayi yanena izi itayendera misewu inayi ya Kenyatta , Mzimba, Crossroads kukafika Ku Kanengo komanso mlatho wa Lilongwe.

A Hara ati pakadali pano zovuta zina zonse zomwe zinachititsa kuti ntchitozi aziimitse kaye m’mbuyomu kaamba ka kuchepa kwa mphanvu ya ndalama ya Kwacha azikonza.

Iwo ati msewu wa Mzimba omwe unali pa K9 billion wafika pa K17 billion ndipo wa Kenyatta omwe unali pa K19 billion wafika pa K35 billion.

A Hara ati cholinga chawo nchoti dziko lino likhale ndi misewu yapamwamba komanso yolimba ndipo ati sakuopa kuika ndalama zochuluka chonchi kuti izi zitheke. Iwo ati ndiokhutira ndi mmene ma kontarakita akuchitira ntchitoyi kaamba koti akutsatira ndondomeko.

 

Related posts

Tumaini Festival clocks 10 years

Romeo Umali

RBM calls for Insurance Act review

Rabson Kondowe

Ndi mlandu kugulitsa, kuononga ndalama zachitsulo — Banki ya Reserve

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.