Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Timu ya Draughts yalephera kupita ku Russia

Timu ya masewero a Draughts ya dziko lino yalephera kupita kukasewera nawo mpikisano wa dziko lonse kaamba kochedwa kukonzekera.

Mlembi wa bungwe loyendetsa masewero wa m’dziko muno la ADIMA, Suzgo Nkhoma, wauza MBC kuti anachedwa kuchititsa mpikisano opeza akatswiri opita ku Russia kaamba kosowa ndalama ndipo izi zachititsa kuti alephere kupangitsa ma VISA a osewerawa mu nthawi  yabwino.

Osewera okwana asanu ndi amene amayenera kupita ku mpikisanowo.

A Nkhoma ati padakali pano, chidwi chonse ayika pa mpikisano wa m’mayiko a mu Africa omwe uchitike mwezi wa November m’dziko la Zimbabwe.

 

Olemba Amin Mussa

Related posts

Stakeholders bang heads over delayed tobacco proceeds payment

Rabson Kondowe

MEC yalengeza zotsatira za chisankho cha komiti yayikulu ya DPP

Rabson Kondowe

Mlembi wamkulu wa Synodi akhetsa msozi ku msonkhano waukulu

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.