Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News Nkhani Politics

Tikambe zabwino za dziko lathu — JB

Mtsogoleri wakale wa dziko lino, Dr Joyce Banda, wapempha a Malawi kuti adzikamba zinthu zabwino zokhudza dziko lino kuti lipite patsogolo.

Dr Banda, omwe ndi mtsogoleri wa chipani cha PP, amayankhula izi pa msonkhano omwe anachititsa pa bwalo la Nancholi m’boma la Blantyre.

Iwo ati aMalawi ambiri akugwiritsa ntchito masamba a mchezo molakwika ponyoza dziko lino, zomwe ati ndi zomvetsa chisoni.

Mtsogoleriyu watinso mavuto a dziko lino kuti athe akufunika m’gwirizano pakati pa boma, zipani za ndale komanso mabungwe omwe si aboma.

Dr Banda anamemanso a Malawi kuti apitilire kugwira ntchito molimbika ndi cholinga chotukula miyoyo yawo.

Olemba: Blessings Cheleuka
#MBCDigital
#Manthu

Related posts

CHAKWERA LEADS MALAWIANS IN CELEBRATING 58 YEARS OF SELF RULE

MBC Online

NICE calls for mindset change in agriculture

MBC Online

‘Adolescents should have access to sexual and reproductive health services’

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.