Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

‘Tidzibweretsa malita 2 million pa ulendo umodzi’

Mkulu wa kampani ya NACALA Logistics, a Chandra Mahon Singh, ati  kuyambira sabata ya mawa adzikwanitsa kubweretsa malita a mafuta okwanira 2 million ndipo ati ali ndikuthekera konyamula mafuta pafupifupi malita 4 million pa ulendo umodzi.

Pakadali pano, a Singh  ati kampaniyi idzinyamula mafutawa pakamodzi pa ulendo wa masiku awiri kuchokera ku Nacara kufika ku Lilongwe.

Iwo ati ntchito yokonza njanji ya Kanengo kupita ku Balaka yatha ndipo apitiriza kukonzanso njanjiyi pakati pa Kanengo ndi Mchinji  kukafika ku Zambia ndipo ntchitoyi itha  m’mwezi wa October.

Iwo ati kmpani yawo ndiyodzipereka kuthandiza boma pa ntchito za mtengatenga, makamaka ponyamula katundu osiyanasiyana.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Parliament to hold open session in Dedza

Sothini Ndazi

Malawi U-17 teams drawn for 2024 COSAFA

MBC Online

Zomba Chingale legislator sent out for violating rules of the House

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.