Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

‘Tidzibweretsa malita 2 million pa ulendo umodzi’

Mkulu wa kampani ya NACALA Logistics, a Chandra Mahon Singh, ati  kuyambira sabata ya mawa adzikwanitsa kubweretsa malita a mafuta okwanira 2 million ndipo ati ali ndikuthekera konyamula mafuta pafupifupi malita 4 million pa ulendo umodzi.

Pakadali pano, a Singh  ati kampaniyi idzinyamula mafutawa pakamodzi pa ulendo wa masiku awiri kuchokera ku Nacara kufika ku Lilongwe.

Iwo ati ntchito yokonza njanji ya Kanengo kupita ku Balaka yatha ndipo apitiriza kukonzanso njanjiyi pakati pa Kanengo ndi Mchinji  kukafika ku Zambia ndipo ntchitoyi itha  m’mwezi wa October.

Iwo ati kmpani yawo ndiyodzipereka kuthandiza boma pa ntchito za mtengatenga, makamaka ponyamula katundu osiyanasiyana.

Related posts

‘Kupapira bibida mwachisawawa kukusokoneza chitukuko’

Romeo Umali

Achisale no more

Romeo Umali

WFP URGES STAKEHOLDERS TO IMPLEMENT CROP INSURANCE POLICIES

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.