Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Tajong atha osasewera nawo Blantyre Derby

Katswiri watsopano womwetsa zigoli wa timu ya Mighty Mukuru Wanderers yemwe kwawo ndi ku Cameroon, Sama Thierry Tajong, ndi wokayikitsa ngati asewere nawo Blantyre Derby kaamba koti sanalandilmrebe chilolezo chosewera mpira kapena kugwira ntchito mdziko muno (Work permit) pa chingerezi.

Kumayambiliro kwa sabata ino, Tanjong anasaina mgwirizano wa zaka ziwiri  ndi timu ya Wanderers.

Padakali pano timu-yi ikuyesetsa  kuti katswiri-yu apeze chilolezo chosewera masewero ake woyamba pomwe Wanderers ikukumana ndi timu ya FCB Nyasa Big Bullets masanawa mu ligi ya TNM.

 

Olemba Amin Mussa

Related posts

PRISAM grants full scholarship to Chaminade’s needy student

McDonald Chiwayula

163,000 candidates to write JCE this year

Romeo Umali

Dr Chakwera apereka ulemu omaliza kwa malemu Dr Chilima ku Nyumba ya Malamulo

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.