Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

PROPHET SHEPHERD BUSHIRI AGAWA CHIMANGA M’MABOMA AKUM’MWERA KUMAPETO ASABATAYI

Ntchito yogawa chimanga chaulere kwa anthu ovutika yomwe akuchita mtsogoleri wa mpingo wa Enlightened Christian Gathering the Jesus Nation  Prophet Shepherd Bushiri ipitilira nchigawo chakummwera kumathero asabatayi mmaboma a Mulanje ndi Thyolo.

Pakadali pano anthu okwana 24000 ndi omwe alandira kale thandizoli m’maboma a Ntcheu ndi Lilongwe.

Ena omwe alandira chimangachi m’boma la Lilongwe.

Polankhula pomwe amakagawa chimangachi m’maboma a Ntcheu ndi Lilongwe,  Prophet Bushiri anati nkofunika  kuti anthu akufuna kwabwino omwe  ali ndi kochepa, agawireko ena powonetsa chikondi chomwe Mulungu amatiphunzitsa.

Lipoti la MVAC,  yemwe ndi kafukufuku wa mmene chakudya chikupezekera m’dziko muno linaonetsa kuti anthu opitilira 4 million ndi omwe akhudzidwa ndi njala chaka chino mdziko muno.

Olemba:  Eunice Ndhlovu.
#mbconlineservices

Related posts

Dr Usi ayamikira mpingo wa Anglican pothandizira boma pa chitukuko

Romeo Umali

‘Anthu achikulire akhale ndi mwayi ovota’

MBC Online

Gulu la alimi lapeza K620 million kudzera mu ulimi wa nzimbe

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.