Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

PROPHET SHEPHERD BUSHIRI AGAWA CHIMANGA M’MABOMA AKUM’MWERA KUMAPETO ASABATAYI

Ntchito yogawa chimanga chaulere kwa anthu ovutika yomwe akuchita mtsogoleri wa mpingo wa Enlightened Christian Gathering the Jesus Nation  Prophet Shepherd Bushiri ipitilira nchigawo chakummwera kumathero asabatayi mmaboma a Mulanje ndi Thyolo.

Pakadali pano anthu okwana 24000 ndi omwe alandira kale thandizoli m’maboma a Ntcheu ndi Lilongwe.

Ena omwe alandira chimangachi m’boma la Lilongwe.

Polankhula pomwe amakagawa chimangachi m’maboma a Ntcheu ndi Lilongwe,  Prophet Bushiri anati nkofunika  kuti anthu akufuna kwabwino omwe  ali ndi kochepa, agawireko ena powonetsa chikondi chomwe Mulungu amatiphunzitsa.

Lipoti la MVAC,  yemwe ndi kafukufuku wa mmene chakudya chikupezekera m’dziko muno linaonetsa kuti anthu opitilira 4 million ndi omwe akhudzidwa ndi njala chaka chino mdziko muno.

Olemba:  Eunice Ndhlovu.
#mbconlineservices

Related posts

Amunjata kaamba koba zipangizo za ESCOM

Romeo Umali

APOLISI KU LIMBE ALONJEZA KUPEREKA CHITETEZO CHOKWANIRA

Alinafe Mlamba

Ogwira mkayidi othawa adzilandira thumba lachimanga

Yamikani Simtowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.