Malawi Broadcasting Corporation
Business Local News Nkhani

‘World Bank ili ndi chikhulupiliro mu utsogoleri ku Malawi’

Mmodzi wa ounikira nkhani za utsogoleri wabwino, Undule Mwakasungula, wayamikira mtsogoleri wa dziko lino, Dr Lazarus Chakwera, pobweretsa chikhulupiliro mwa a World Bank pamene yapereka K613 billion yomangira malo opangira mphamvu za magetsi a Mpatamanga m’boma la Blantyre.

A Mwakasungula ati ntchitoyi ikadzatha idzachititsa dziko lino kukhala ndi mphamvu za magetsi zodalirika, zomwenso angadzamagulitse m’mayiko ena.

Iwo ati ma ulamuliro ena mmbuyomu akhala akusakaza ndalama zoterezi, zimene zapangitsa dziko la Malawi kukhala ndi mavuto ochuluka m’magawo osiyanasiyana.

Iwo alangiza boma kuti ndalamazi zigwire ntchito yoyenera.

Olemba: Blessings Cheleuka

Related posts

Scottish Govt launches Climate Justice Initiative in Malawi

Romeo Umali

Galimoto 40 zonyamula mafuta zafika m’dziko muno, zinanso 70 zifika – NOCMA

Rabson Kondowe

Mponda vs. Mgangira: Master faces apprentice

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.