Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Prezidenti Chakwera acheza ndi anthu pa Nanyumbu ku Machinga

Prezidenti Dr Lazarus Chakwera wati zokambirana zimene anali nazo ndi mafumu aku Machinga zayenda bwino.

Dr Chakwera watsimikizira anthu a m’bomali kuti ali ndi chidwi potukula nkhani zaulimi m’dziko muno kuti aliyense adzikhala ndi chakudya chokwanira.

Mtsogoleriyu wayamikira ntchito imene ikuchitika ku scheme ya Mlooka, kumene ulimi wanthilira ukuchitidwa pogwiritsa ntchito mphamvu yadzuwa komanso makina amakono.

Polankhulapo pankhani ya magetsi, Dr Chakwera anati ndi khumbo lake kuti magetsi afikire paliponse mdziko muno, maka mmadera akumidzi.

Potsiliza, mtsogoleri wadziko linoyu walangiza makolo kuti alimbikitse ana awo pankhani ya maphunziro kuti adzakhale odzidalira mtsogolo.

Related posts

Sing’anga akakhala kundende pamlandu ogwililira

Rabson Kondowe

MEC impressed by progress of 3rd phase voter registration

Romeo Umali

President Chakwera akayendera ntchito zachitukuko kumpoto

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.